Unali wanga zione

Cholichose ndimapanga kuti chikondi kwaiwe ndikupanga

Nthawi zonse palipose ndimakhala ndiiwe

Nyengo iliyose pa chilichose ndimakhala nawe

Koma zonsezi zinaphula palibe poti wachikondi pano ndilibe

Unali wanga wanga amadziwaso anzanga

Kumbuka Zione zomwe iwe ndiine tapanga

Mokunyadira ndinkukutchula kuti akazi anga

Koma kundisiya ndekha padzuwa ndi zomwe wasankha kupanga

Unali wapamtima wanga Zione

Kwa ena ngati Kalulu kwa galu ndinali m’dani chifukwa Cha iwe

Ndimalora kuthawa anzanga kuti ndisangalatse iwe

Inde,kuyesetsa kukukonda iwe

Koma palumbe kundisiya, Moti izi ndi mbiri chabe unali wanga Zione