Mkazi wanga Pede chilungamo ndiuze

Ngati pathupi ulinapo ndi panga

Poti sindikumvetsa zomwe ukupanga

Ndiwe mkazi wanga kapena wa mnzanga?

Pede yankhula zoona ngati ndilipo ndekha

Ukutha masiku ambiri kunja ine ndili ndekha

Kumapita kukajowa ziimbilo ine ndili ndekha

Yankhule Pede sindikufuna kudzidabwitsa ndekha

Pede duwa langa iwe

Kodi alipo angati othilira duwa iwe?

Dzulo ndakupeza ndi mphongo yakwa Chiphazi

Lero kukupeza ndi Wina wakwa Nthazi