Mtima wanga dekha

Poti aka sikoyamba kugwa mchikondi

Kumbuka padzana kuti achikondi opanda choona chikondi udali nawo mchikondi

Ndipo achikondi a chabodza chikondi udawapatsa choona chikondi

Koma zonsezi zidakuliza ngati iwe sudali mchikondi

Mchifukwa chake ndikuti dekha mtima wanga izi ndizachikondi

Dekha iwe wanga mtima

Aka sikoyamba kuuzidwa kuti ndiwe wake wapamtima

Kumbukatu yako nambala ankanena pamtima

Ndipo ankati amamva phalombe akakhala pako pamtima

Komatu onsewa anakuswa kumbuka wanga mtima

Choncho dekha usakhale ndi phuma wanga mtima

Usapupulume wanga mtima

Aka sikoyamba kuuzidwa kuti umakondedwa

Kumbuka dzulo dzulo analipo ngati awa okondedwa

Kuti mpaka muyaya sudzasiidwa iwe unauzidwa

Kutiso mpaka kale udzakondedwa unauzidwa

Komatu zonsezi unanamizidwa

Ndipo sichinali chikondi koma kuzuzidwa

Mokupempha dekha mtima wanga

Aka sikoyamba kulonjezedwa ndi wokondedwa

Kumbuka kuti adzakutengera kwawo udzauzidwa

Kutiso zamwano sudzayankhidwa udauzidwa

Nde nanga kwawoko udatengeredwa?

Nanga mwano sukuyankhidwa?

Chonde mtima wanga dekha kuopa kachikena kunamizidwa

Dekha mtima wanga ndagwira mwendo wako

Poti aka sikoyamba kuuzidwa kuti Nyagondwe ndi wako wako

Kumbuka dzulo lija Chepatuma ankati ndi wako wako

Ndipo Nachisare ndi Nyakumwenda adaliso ako ako

Nanga matsuna onsewa akadali ako?

Kodi ziphadzuwa zija ndi azimai aana ako?

Onsewa anakusiya ndiye dekha chonde usamangojijilikapo