Mwanawe kuti dzikoli lisadzakuwawe

Zinthu zoipa zadzikoli mwadala usazilawe

Bibida, jang’ala , hona ndi ambuye mtengeni usadzalawe

Poti ukatero ndeti ukufuna dzikoli kuwawa udzalimve

Mwanawe dekha dziko ndilomvuta

Anthu amdzikoli mmm ndiovuta

Zibwana dala usapange

Njuga ndi uhule chonde usamapange

Mwanawe usanyalanyaze anga malangizo

Nthawi zonse uzimvera abwino malangizo

Ndipo ukatero wadziko sudzauva ululu

Poti dzikoli ndi Chibwana ndi galu ndi kalulu